Aheberi 1:1-14
1 Kalekale, Mulungu analankhula ndi makolo athu nthawi zambiri+ ndiponso m’njira zambiri kudzera mwa aneneri.+
2 Kumapeto kwa masiku ano,+ iye walankhulanso kwa ife kudzera mwa Mwana wake,+ amene anamuika kuti akhale wolandira zinthu zonse monga cholowa.+ Kudzera mwa iyeyu, Mulungu analenga+ nthawi* zosiyanasiyana.
3 Iye amasonyeza ndendende mmene ulemerero wa Mulungu ulili+ ndipo ndiye chithunzi chenicheni cha Mulungu weniweniyo,+ ndipo amachirikiza zinthu zonse mwa mawu ake amphamvu.+ Atatiyeretsa potichotsera machimo athu,+ anakhala pansi kudzanja lamanja+ la Wolemekezeka m’malo okwezeka.+
4 Choncho iye wakhala woposa angelo,+ moti monga cholowa chake, walandira dzina+ lapamwamba kwambiri kuposa lawo.
5 Mwachitsanzo, kodi Mulungu anauzapo mngelo uti kuti: “Iwe ndiwe mwana wanga. Lero ine ndakhala atate wako”?+ Kapena kuti: “Ine ndidzakhala atate wake ndipo iye adzakhala mwana wanga”?+
6 Koma ponena za nthawi imene adzatumize kachiwiri Mwana wake Woyamba kubadwayo+ padziko lapansi kumene kuli anthu, iye akuti: “Angelo+ onse a Mulungu amugwadire.”+
7 Ndiponso ponena za angelo, iye akuti: “Amapanga angelo ake kukhala mizimu, ndipo amapanganso antchito ake otumikira ena kukhala lawi la moto.”+
8 Koma ponena za Mwana wake, iye akuti: “Mulungu ndiye mpando wako wachifumu mpaka muyaya,+ ndipo ndodo ya ufumu+ wako ndiyo ndodo yachilungamo.+
9 Unakonda chilungamo ndipo unadana ndi kusamvera malamulo. N’chifukwa chake Mulungu, Mulungu wako, anakudzoza+ ndi mafuta achikondwerero chachikulu kuposa cha mafumu ena.”+
10 Iye akunenanso kuti: “Inu Ambuye, pachiyambipo munaika maziko a dziko lapansi, ndipo kumwamba ndiko ntchito ya manja anu.+
11 Zimenezi zidzatha, koma inu mudzakhalapo mpaka muyaya. Ndipo zonsezi zidzatha ngati mmene malaya akunja amathera.+
12 Mudzapindapinda zinthu zimenezi ngati mkanjo,+ ndipo zidzasinthidwa ngati malaya akunja. Koma inu simudzasintha, ndipo zaka za moyo wanu sizidzatha.”+
13 Koma kodi ndi mngelo uti amene anamuuzapo kuti: “Khala kudzanja langa lamanja, kufikira nditaika adani ako monga chopondapo mapazi ako”?+
14 Kodi angelo onse si mizimu+ yotumikira ena,+ yotumidwa kukatumikira amene adzalandire chipulumutso monga cholowa chawo?+
Mawu a M'munsi
^ Onani Matanthauzo a Mawu Ena.