Agalatiya 6:1-18

6  Abale, ngati munthu wapatuka n’kuyamba kulowera njira yolakwika+ mosazindikira, inu oyenerera mwauzimu,+ yesani kumuthandiza munthu woteroyo ndi mzimu wofatsa.+ Pamene mukutero, aliyense wa inu asamale,+ kuopera kuti iyenso angayesedwe.+  Musaleke kunyamulirana zolemetsa.+ Mukatero mudzakhala mukukwaniritsa chilamulo cha Khristu.+  Pakuti ngati wina akudziona kuti ndi wofunika pamene si wotero,+ akudzinyenga.  Koma aliyense payekha ayese ntchito yake, kuti aone kuti ndi yotani.+ Akatero adzakhala ndi chifukwa chosangalalira ndi ntchito yake, osati modziyerekezera+ ndi munthu wina.  Pakuti aliyense ayenera kunyamula katundu wake.+  Komanso, aliyense amene akuphunzitsidwa mawuwo+ agawane+ zinthu zonse zabwino ndi amene akumuphunzitsayo.+  Musanyengedwe,+ Mulungu sapusitsika.+ Chilichonse chimene munthu wafesa, adzakololanso chomwecho.+  Pakuti amene akufesa ndi cholinga chopindulitsa thupi lake, adzakolola chiwonongeko kuchokera m’thupi lakelo,+ koma amene akutsatira mzimu wa Mulungu+ adzakolola moyo wosatha kuchokera ku mzimuwo.+  Choncho tisaleke kuchita zabwino,+ pakuti pa nyengo yake tidzakolola tikapanda kutopa.+ 10  Chotero ngati tingathe,+ tiyeni tichitire onse zabwino, koma makamaka abale ndi alongo athu m’chikhulupiriro.+ 11  Taonani zilembo zikuluzikulu zimene ndakulemberani ndekha ndi dzanja langali.+ 12  Onse ofuna kudzionetsa ngati abwino pamaso pa anthu ndi amene akukuumirizani kuti muzidulidwa.+ Akuchita zimenezi kuti asazunzidwe chifukwa cha mtengo wozunzikirapo wa Khristu,+ amene ndi Yesu. 13  Pakuti ngakhale amene akudulidwawo sasunga Chilamulo,+ koma akufuna inuyo mudulidwe kuti iwo azidzitama chifukwa cha zimene zachitika pathupi lanu. 14  Ineyo sindidzadzitama pa chifukwa china chilichonse, koma chifukwa cha mtengo wozunzikirapo+ wa Ambuye wathu Yesu Khristu basi. Kudzera mwa ameneyu, kwa ine dziko lapansi lapachikidwa, ndipo malinga ndi kuona kwa dziko lapansi,+ ineyo ndapachikidwa. 15  Pakuti kudulidwa kapena kusadulidwa si kanthu,+ koma chofunika ndi kukhala wolengedwa mwatsopano.+ 16  Ndipo onse otsatira lamulo limeneli la mmene tiyenera kukhalira, amene ndi Isiraeli wa Mulungu, akhale ndi mtendere ndiponso chifundo.+ 17  Kuyambira tsopano, pasapezeke munthu wondivutitsa, pakuti thupi langali lili ndi zipsera za chizindikiro+ cha kapolo wa Yesu.+ 18  Abale, kukoma mtima kwakukulu kwa Ambuye wathu Yesu Khristu, kukhale nanu chifukwa cha mzimu+ umene mumausonyeza. Ame.

Mawu a M'munsi