2 Samueli 22:1-51

22  Davide analankhula ndi Yehova mawu a nyimbo iyi,+ pa tsiku limene Yehova anamulanditsa kwa adani ake+ onse ndiponso m’manja mwa Sauli.+  Iye anati:“Yehova ndiye thanthwe langa,+ malo anga achitetezo+ ndiponso Wopereka chipulumutso kwa ine.+   Mulungu wanga ndiye thanthwe langa.+ Ine ndidzathawira kwa iye,Iye ndi chishango changa,+ nyanga* yanga+ ya chipulumutso ndi malo anga okwezeka achitetezo.+Iye ndi malo anga othawirako,+ Mpulumutsi wanga.+ Mumandipulumutsa ku chiwawa.+   Ndidzaitanira pa Yehova, Iye woyenera kutamandidwa,+Ndipo adzandipulumutsa kwa adani anga.+   Pakuti mafunde akupha anandizungulira.+Panali chikhamu cha anthu opanda pake amene anali kundiopseza.+   Zingwe za Manda* zinandizungulira.+Ndinakumana ndi misampha ya imfa.+   Pa nthawi ya zowawa zanga ndinaitana Yehova,+Ndinaitana Mulungu wanga.+Pamenepo iye anamva mawu anga ali m’kachisi wake,+Makutu ake anamva kulira kwanga kopempha thandizo.+   Dziko lapansi linayamba kugwedezekera uku ndi uku ndiponso kutekeseka.+Maziko a kumwamba anagwedezeka.+Anagwedezekera uku ndi uku chifukwa Mulungu anakwiya.+   Utsi unatuluka m’mphuno mwake, ndipo moto wotuluka m’kamwa mwake unanyeketsa.+Makala onyeka anatuluka mwa iye.+ 10  Iye anaweramitsa kumwamba n’kutsika.+Mdima wandiweyani unali kunsi kwa mapazi ake.+ 11  Iye anafika atakwera pakerubi+ wouluka.Anaonekera pamapiko a cholengedwa chauzimu.*+ 12  Kenako anaika mdima momuzungulira ngati misasa,+Anaika madzi akuda ndi mtambo wakuda.+ 13  M’kuwala kochokera pamaso pake munatuluka makala oyaka moto.+ 14  Ali kumwamba, Yehova anayamba kugunda ngati mabingu,+Wam’mwambamwamba anayamba kutulutsa mawu ake.+ 15  Anayamba kuponya mivi kuti awabalalitse.+Anaponya mphezi kuti awasokoneze.+ 16  Ndipo ngalande za pansi pa nyanja zinaonekera,+Maziko a dziko lapansi+ anakhala poonekera,Zinatero chifukwa cha kudzudzula kwa Yehova, chifukwa cha mphamvu ya mpweya wa m’mphuno mwake.+ 17  Anatambasula dzanja lake kuchokera kumwamba ndi kunditenga,+Anandivuula m’madzi akuya.+ 18  Anandilanditsa kwa mdani wanga wamphamvu,+Anandilanditsa kwa odana nane chifukwa anali amphamvu kuposa ine.+ 19  Adaniwo anandifikira m’tsiku la tsoka langa,+Koma Yehova anandichirikiza.+ 20  Ananditenga ndi kundiika pamalo otakasuka.+Anandipulumutsa chifukwa anakondwera nane.+ 21  Yehova amandipatsa mphoto mogwirizana ndi chilungamo changa.+Amandibwezera mogwirizana ndi kuyera kwa manja anga.+ 22  Pakuti ndasunga njira za Yehova,+Sindinachoke kwa Mulungu wanga.+ Ndikanatero, ndikanachita chinthu choipa. 23  Pakuti zigamulo+ zake zonse zili pamaso panga.Ndipo sindidzapatuka pa malamulo ake.+ 24  Ndidzakhalabe wopanda cholakwa+ pamaso pake,Ndipo ndidzayesetsa kupewa cholakwa.+ 25  Yehova andibwezere mogwirizana ndi chilungamo changa,+Andibwezere mogwirizana ndi kukhala kwanga woyera pamaso pake.+ 26  Munthu wokhulupirika, mudzamuchitira mokhulupirika.+Munthu wamphamvu wopanda cholakwa, mudzamuchitira mwachilungamo.+ 27  Kwa munthu wokhalabe woyera, mudzadzisonyeza kuti ndinu woyera,+Kwa munthu wopotoka maganizo mudzachita zinthu ngati wopusa.+ 28  Anthu odzichepetsa mudzawapulumutsa.+Koma mumatsutsa odzikweza, kuti muwatsitse.+ 29  Inu Yehova ndinu nyale yanga,+Ndipo Yehova ndiye amandiunikira pamene ndili mu mdima.+ 30  Pakuti ndi thandizo lanu ndingathamangitse gulu la achifwamba.+Ndi thandizo la Mulungu wanga ndingakwere khoma.+ 31  Njira ya Mulungu woona ndi yangwiro.+Mawu a Yehova ndi oyengeka bwino.+Iye ndi chishango kwa onse othawira kwa iye.+ 32  Kodi pali Mulungu winanso woposa Yehova?+Kodi pali thanthwe linanso loposa Mulungu wathu?+ 33  Mulungu woona ndiye malo anga otetezeka kwambiri,+Ndipo adzasalaza njira yanga.+ 34  Iye adzachititsa mapazi anga kukhala aliwiro ngati a mbawala zazikazi,+Ndipo adzandiimiritsabe pamalo okwezeka kwa ine.+ 35  Iye akuphunzitsa manja anga kumenya nkhondo.+Ndipo manja anga akukunga uta wamkuwa.+ 36  Inu mudzandipatsa chishango chanu cha chipulumutso,+Ndipo kudzichepetsa kwanu n’kumene kumandikweza.+ 37  Mudzakulitsa malo opondapo mapazi anga.+Ndipo mapazi anga sadzagwedezeka.+ 38  Ndidzathamangitsa adani anga kuti ndiwafafanize,Ndipo sindidzabwerera kufikira nditawawononga onse.+ 39  Ndidzawawononga onse ndi kuwaphwanya zibenthuzibenthu+ kuti asadzukenso.+Iwo adzagwa pansi ndipo ndidzawapondaponda ndi mapazi anga.+ 40  Inu mudzandiveka mphamvu kuti ndithe kumenya nkhondo.+Mudzakomola ondiukira.+ 41  Koma mudzachititsa adani anga kugonja* pamaso panga,+Anthu odana nane kwambiri, ndidzawakhalitsa chete.+ 42  Adzafuula kupempha thandizo, koma sipadzapezeka wowapulumutsa,+Adzafuulira Yehova, koma sadzawayankha.+ 43  Ndidzawapera kukhala ngati fumbi la padziko lapansi.Ndidzawapondaponda ngati matope a mumsewu,+Ndipo ndidzawasasantha. 44  Inu mudzandipulumutsa kwa anthu a mtundu wanga onditola zifukwa.+Mudzanditeteza kuti ndikhale mtsogoleri wa mitundu yonse.+Anthu amene sindikuwadziwa adzanditumikira.+ 45  Alendo adzabwera kwa ine akunthunthumira.+Anthu adzamvetsera mawu anga ndi kuwatsatira.+ 46  Alendo adzatha mphamvu,Ndipo adzatuluka m’malo awo achitetezo akunjenjemera.+ 47  Yehova ndi wamoyo.+ Lidalitsike Thanthwe langa.+Mulungu wanga, thanthwe limene limandipulumutsa likhale lokwezeka.+ 48  Mulungu woona ndiye Wobwezera adani anga,+Iye amaika mitundu ya anthu kunsi kwa mapazi anga.+ 49  Iye amandichotsa pakati pa adani anga.+Ndipo mudzandikweza pamwamba pa anthu amene amandiukira.+Mudzandilanditsa kwa munthu wochita zachiwawa.+ 50  N’chifukwa chake ndidzayamika inu Yehova pakati pa mitundu.+Ndipo ndidzaimba nyimbo zotamanda dzina lanu.+ 51  Ndidzaimbira Iye wochita ntchito zazikulu zachipulumutso kwa mfumu yake,+Iye wosonyeza kukoma mtima kosatha kwa wodzozedwa wake,+Kwa Davide ndi mbewu yake mpaka kalekale.”+

Mawu a M'munsi

Onani mawu a m’munsi pa 1Sa 2:1.
Onani Zakumapeto 5.
Kapena kuti “mapiko a mphepo.”
Kapena kuti, “Mudzandipatsa kumbuyo kwa khosi la adani anga.”