2 Akorinto 4:1-18
4 Popeza tili ndi utumiki umenewu+ malinga ndi chifundo chimene tinasonyezedwa,+ sitikubwerera m’mbuyo.
2 Koma tasiya zinthu zochititsa manyazi zochitikira mseri,+ ndipo sitikuyenda mwachinyengo komanso sitikupotoza mawu a Mulungu.+ Koma pamaso pa Mulungu, takhala chitsanzo chabwino kwa chikumbumtima cha munthu aliyense.+
3 Tsopano ngati uthenga wabwino umene tikulengeza uli wophimbika, ndi wophimbika pakati pa anthu amene akupita kukawonongedwa.+
4 Pakati pa anthu amenewa, mulungu wa nthawi* ino+ wachititsa khungu maganizo a anthu osakhulupirira,+ kuti asaone+ kuwala+ kwa uthenga wabwino waulemerero+ wonena za Khristu, yemwe ali chifaniziro+ cha Mulungu.
5 Pakuti sitikulalikira za ifeyo koma za Khristu Yesu, kuti iye ndiye Ambuye+ ndipo ifeyo ndife akapolo+ anu chifukwa cha Yesu.
6 Pakuti Mulungu ndiye anati: “Kuwala kuunike kuchokera mu mdima,”+ ndipo kudzera mwa nkhope ya Khristu,+ waunika mitima yathu kuti iwale+ ndi ulemerero wokhudzana ndi kudziwa+ Mulungu.
7 Komabe, tili ndi chuma+ chimenechi m’zonyamulira+ zoumbidwa ndi dothi,+ kuti mphamvu+ yoposa yachibadwa ichokere kwa Mulungu,+ osati kwa ife.+
8 Timapanikizidwa mwamtundu uliwonse,+ koma osati kupsinjidwa moti n’kulephera kusuntha. Timathedwa nzeru, koma osati mochita kusoweratu pothawira.+
9 Timazunzidwa, koma osati mochita kusowa kolowera.+ Timagwetsedwa pansi,+ koma sitiwonongedwa.+
10 Kulikonse kumene tikupita, timapirira m’matupi mwathu ndipo timakhala pa ngozi yoti tikhoza kuphedwa, ngati mmene Yesu anachitira,+ kuti moyo wa Yesu uonekerenso m’matupi mwathu.+
11 Pakuti nthawi zonse amoyofe timakhala pa ngozi yoti tikhoza kuphedwa+ chifukwa cha Yesu, kuti moyo wa Yesu uonekerenso m’thupi lathu lokhoza kufali.+
12 Choncho ngakhale kuti moyo wathu ukukhala pa ngozi, zimenezi zikubweretsa moyo kwa inuyo.+
13 Tsopano, popeza tili ndi mtima wachikhulupiriro wofanana ndi umene anaunena kuti: “Ndinali ndi chikhulupiriro, chotero ndinalankhula,”+ ifenso tili ndi chikhulupiriro, chotero tikulankhula,
14 podziwa kuti amene anaukitsa Yesu adzaukitsanso ifeyo pamodzi ndi Yesu, ndipo adzatipititsa pamaso pa Yesuyo pamodzi ndi inuyo.+
15 Pakuti zonsezi zachitika chifukwa cha ubwino wanu.+ Ndiponso zachitika kuti kukoma mtima kwakukulu kumene kunawonjezeka kuchulukebe chifukwa cha anthu ambiri amene akupereka mapemphero oyamikira, zimene zikuchititsa kuti Mulungu alandire ulemerero.+
16 Choncho sitikubwerera m’mbuyo. Koma ngakhale munthu wathu wakunja akutha, ndithudi munthu wathu wamkati+ akukhalitsidwanso watsopano tsiku ndi tsiku.
17 Pakuti ngakhale kuti masautso amene tikukumana nawo ndi akanthawi+ ndipo ndi opepuka, masautsowo akutichititsa kuti tilandire ulemerero umene ukukulirakulira komanso wamuyaya,+
18 pamene tikuika maso athu pa zinthu zosaoneka, osati pa zooneka.+ Pakuti zooneka n’zakanthawi,+ koma zosaoneka n’zamuyaya.+
Mawu a M'munsi
^ Onani Matanthauzo a Mawu Ena.