1 Atesalonika 5:1-28

5  Koma tsopano za nthawi ndi nyengo+ abale, simukufunika kukulemberani kanthu.  Pakuti inu eni mukudziwa bwino kuti tsiku la Yehova*+ lidzabwera ndendende ngati mbala usiku.+  Pamene azidzati:+ “Bata ndi mtendere!”+ chiwonongeko+ chodzidzimutsa chidzafika pa iwo nthawi yomweyo monga zowawa za pobereka za mkazi wapakati,+ ndipo sadzapulumuka.+  Koma inu abale simuli mu mdima ayi,+ kuti tsiku limenelo lidzakudzidzimutseni ngati mmene lingachitire kwa mbala.+  Pakuti inu nonse ndinu ana a kuwala+ ndiponso ana a usana.+ Si ife a usiku kapena a mdima ayi.+  Chotero tisapitirize kugona+ ngati mmene enawo akuchitira,+ koma tikhalebe maso+ ndipo tikhalebe oganiza bwino.+  Pakuti ogona+ amagona usiku,+ ndipo amene amaledzera amakonda kuledzera usiku.  Koma ife amene tili a usana, tikhalebe oganiza bwino ndipo tivale chodzitetezera pachifuwa+ chachikhulupiriro+ ndi chikondi. Tivalenso chiyembekezo chachipulumutso+ monga chisoti,+  chifukwa Mulungu sanatisankhe kuti tidzaone mkwiyo.+ Anatisankha kuti tipeze chipulumutso+ kudzera mwa Ambuye wathu Yesu Khristu.+ 10  Iye anatifera,+ kuti kaya tikhala maso kapena tigona, tikhale ndi moyo limodzi ndi iye.+ 11  Choncho pitirizani kutonthozana ndi kulimbikitsana+ monga mmene mukuchitira.+ 12  Tsopano tikukupemphani abale, kuti muzilemekeza anthu amene akugwira ntchito mwakhama pakati panu, amenenso amakutsogolerani+ mwa Ambuye ndi kukulangizani. 13  Muwapatse ulemu waukulu mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo.+ Khalani mwamtendere pakati panu.+ 14  Komanso tikukudandaulirani abale kuti, langizani ochita zosalongosoka,+ lankhulani molimbikitsa kwa amtima wachisoni,+ thandizani ofooka, khalani oleza+ mtima kwa onse. 15  Onetsetsani kuti wina asabwezere choipa pa choipa kwa wina aliyense,+ koma nthawi zonse yesetsani kuchita zabwino kwa okhulupirira anzanu ndi kwa ena onse.+ 16  Muzikhala okondwera nthawi zonse.+ 17  Muzipemphera mosalekeza.+ 18  Muziyamika+ pa chilichonse, pakuti chimenechi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu. 19  Musazimitse moto wa mzimu.+ 20  Musanyoze mawu aulosi.+ 21  Tsimikizirani zinthu zonse.+ Gwirani mwamphamvu chimene chili chabwino.+ 22  Pewani zoipa zamtundu uliwonse.+ 23  Mulungu wamtendere+ mwiniyo akupatuleni+ kuti muchite utumiki wake. Ndipo m’mbali zonse abale, mzimu wanu, moyo wanu, ndi thupi lanu, zisungidwe zopanda chilema ndi zopanda cholakwa chilichonse, pa nthawi ya kukhalapo* kwa Ambuye wathu Yesu Khristu.+ 24  Amene akukuitanani ndi wokhulupirika, ndipo adzachitadi zimenezi. 25  Abale, pitirizani kutipempherera.+ 26  Perekani moni kwa abale onse ndi kupsompsonana kwaubale.+ 27  Ndikukulamulani mwa Ambuye kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.+ 28  Kukoma mtima kwakukulu+ kwa Ambuye wathu Yesu Khristu kukhale nanu.

Mawu a M'munsi

Onani Zakumapeto 2.
Onani Zakumapeto 8.